34
Chiweruzo cha Anthu a Mitundu Yonse
Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve:
tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse:
Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo,
dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse;
wapsera mtima magulu awo onse ankhondo.
Iye adzawawononga kotheratu,
nawapereka kuti aphedwe.
Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja,
mitembo yawo idzawola ndi kununkha;
mapiri adzafiira ndi magazi awo.
Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka
ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala;
nyenyezi zonse zidzayoyoka
ngati masamba ofota a mphesa,
ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
 
Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba;
taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu,
anthu amene ndawawononga kotheratu.”
Lupanga la Yehova lakhuta magazi,
lakutidwa ndi mafuta;
magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi,
mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna.
Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira
ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati,
ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe.
Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha,
ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
 
Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira
ndi kulanga adani a Ziyoni.
Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula,
ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule;
dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana;
utsi wake udzafuka kosalekeza.
Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado;
palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu;
amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo.
Mulungu adzatambalitsa pa Edomu
chingwe choyezera cha chisokonezo
ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko;
akalonga ake onse adzachotsedwa.
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa,
khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake.
Ankhandwe azidzadya mʼmenemo;
malo okhalamo akadzidzi.
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi,
ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana.
Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa
ndi kupeza malo opumulirako.
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira,
adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake;
akamtema adzasonkhananso kumeneko,
awiriawiri.
16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga:
mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa;
sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake.
Pakuti Yehova walamula kuti zitero,
ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
17 Yehova wagawa dziko lawo;
wapatsa chilichonse chigawo chake.
Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya
ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.