55
Kuyitanidwa kwa Womva Ludzu
“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu,
bwerani madzi alipo;
ndipo inu amene mulibe ndalama
bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye!
Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka
osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya,
ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa?
Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino;
ndipo mudzisangalatse.
Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine;
mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo.
Ndidzachita nanu pangano losatha,
chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu,
kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa,
ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu.
Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu,
Woyerayo wa Israeli,
wakuvekani ulemerero.”
 
Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka.
Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa,
ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa.
Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo,
ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
 
“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu,
ngakhale njira zanu si njira zanga,”
akutero Yehova.
“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi,
momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu,
ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
10 Monga mvula ndi chisanu chowundana
zimatsika kuchokera kumwamba,
ndipo sizibwerera komweko
koma zimathirira dziko lapansi.
Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera
kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga.
Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake,
koma adzachita zonse zimene ndifuna,
ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
12 Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe
ndipo adzakutsogolerani mwamtendere;
mapiri ndi zitunda
zidzakuyimbirani nyimbo,
ndipo mitengo yonse yamʼthengo
idzakuwombereni mʼmanja.
13 Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini,
ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu.
Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova,
ngati chizindikiro chamuyaya,
chimene sichidzafafanizika konse.”