66
Chiweruzo ndi Chiyembekezo
Yehova akuti,
“Kumwamba ndi mpando wanga waufumu
ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga.
Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire,
ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi,
motero zonsezi ndi zanga?”
Akutero Yehova.
 
“Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu:
amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima,
ndipo amamvera mawu anga.
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna
amaphanso munthu,
ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa,
amaphanso galu.
Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya
amaperekanso magazi a nkhumba.
Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso
amapembedzanso fano.
Popeza iwo asankha njira zawozawo,
ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
Inenso ndawasankhira chilango chowawa
ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija.
Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha,
pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu.
Anachita zoyipa pamaso panga
ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
 
Imvani mawu a Yehova,
inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake:
“Abale anu amene amakudani,
ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti,
‘Yehova alemekezeke
kuti ife tione chimwemwe chanu!’
Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Imvani mfuwu mu mzinda,
imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu!
Limenelo ndi liwu la Yehova,
kulanga adani ake onse.
 
“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa
wachira kale;
asanayambe kumva ululu,
wabala kale mwana wamwamuna.
Ndani anamvapo zinthu zoterezi?
Ndani anazionapo zinthu zoterezi?
Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi,
kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi?
Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa
nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira,
koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova.
“Kodi ndingatseke mimba
pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye,
inu nonse amene mumakonda Yerusalemu,
kondwera nayeni kwambiri,
nonse amene mumamulira.
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake
ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri
wa mʼmawere
a chitonthozo chake.”
12 Yehova akuti,
“Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi,
ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira.
Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa,
kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo,
moteronso Ine ndidzakusangalatsani;
ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
 
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu.
Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu.
Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira
ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto,
ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu;
Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake
ndi malawi amoto.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse
ndi moto ndi lupanga,
Yehova adzapha anthu ambiri.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina. 20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo. 21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova. 23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova. 24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”