40
Mawu a Chitonthozo kwa Anthu a Mulungu
Atonthozeni, atonthozeni anthu anga,
akutero Mulungu wanu.
Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu
ndipo muwawuzitse
kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha,
tchimo lawo lakhululukidwa.
Ndawalanga mokwanira
chifukwa cha machimo awo onse.
 
Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti,
“Konzani njira ya Yehova
mʼchipululu;
wongolani njira zake;
msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
Chigwa chilichonse achidzaze.
Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse;
Dziko lokumbikakumbika alisalaze,
malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera,
ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona,
pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
 
Wina ananena kuti, “Lengeza.”
Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani?
 
“Pakuti anthu onse ali ngati udzu
ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota
chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.”
Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota,
koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
 
Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni,
kwera pa phiri lalitali.
Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu,
fuwula kwambiri,
kweza mawu, usachite mantha;
uza mizinda ya ku Yuda kuti,
“Mulungu wanu akubwera!”
10 Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu,
ndipo dzanja lake likulamulira,
taonani akubwera ndi mphotho yake
watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
11 Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa:
Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake
ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake
ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
 
12 Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake,
kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake?
Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu,
kapena kuyeza kulemera kwa
mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
13 Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova
kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
14 Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya,
kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru?
Iye anapempha nzeru kwa yani
ndi njira ya kumvetsa zinthu?
 
15 Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko.
Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo;
mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
16 Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe,
ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
17 Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake;
Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu
ndi cha chabechabe.
 
18 Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani?
Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
19 Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga
ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide
naliveka mkanda wasiliva.
20 Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere
amasankha mtengo umene sudzawola,
nafunafuna mʼmisiri waluso woti
amupangire fano limene silingasunthike.
 
21 Kodi simukudziwa?
Kodi simunamve?
Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe?
Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
22 Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi,
Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala.
Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga,
nayikunga ngati tenti yokhalamo.
23 Amatsitsa pansi mafumu amphamvu
nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
24 Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene
kapena kufesedwa chapompano,
ndi kungoyamba kuzika mizu kumene
ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa
ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
 
25 Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani?
Kapena kodi alipo wofanana nane?”
26 Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani.
Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi?
Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo,
nayitana iliyonse ndi dzina lake.
Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri,
palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
 
27 Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena
ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti,
“Yehova sakudziwa mavuto anga,
Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
28 Kodi simukudziwa?
Kodi simunamve?
Yehova ndiye Mulungu wamuyaya,
ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi.
Iye sadzatopa kapena kufowoka
ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
29 Iye amalimbitsa ofowoka
ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
30 Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka,
ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
31 koma iwo amene amakhulupirira Yehova
adzalandira mphamvu zatsopano.
Adzawuluka ngati chiwombankhanga;
adzathamanga koma sadzalefuka,
adzayenda koma sadzatopa konse.